19 Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.
20 Ndipo wa Alevi, Ahiya anayang'anira cuma ca nyumba ya Mulungu, ndi cuma ca zopatulika.
21 Ana a Ladani: ana a Ladani a Agerisoni, akuru a nyumba za makolo a Ladani Mgerisoni, Yehieli.
22 Ana a Yehieli: Zetamu ndi Yoeli mbale wace, oyang'anira cuma ca nyumba ya Yehova.
23 A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;
24 ndi Sebueli mwana wa Gerisomu, mwana wa Mose, ndiye mkuru woyang'anira zuma.
25 Ndi abale ace a Eliezeri: Rehabiya mwana wace, ndi Yesava mwana wace ndi Yorramu mwana wace, ndi Zikiri mwana wace, ndi Selomoti mwana wace.