27 ndi woyang'anira minda yamphesa ndiye Simeyi Mramati; ndi woyang'anira zipatso za minda yamphesa zisungike mosungiramo vinyo ndiye Zabidi Msifimi;
28 ndi woyang'anira mitengo yaazitona, ndi yamikuyu yokhala kuzidikha kunsi, ndiye Baala Hanani Mgederi; ndi woyang'anira zosungiramo mafuta ndiye Yoasi;
29 ndi woyang'anira ng'ombe zakudya m'Saroni ndiye Sitirai Msaroni; ndi woyang'anira ng'ombe za m'zigwa ndiye Safabi mwana wa Adilai;
30 ndi woyang'anira ngamira ndiye Obili M-israyeli; ndi woyang'anira aburu ndiye Yedeya Mmeronoti;
31 ndi woyang'anira zoweta zazing'ono ndiye Yazizi Mhagiri, Onsewa ndiwo akuru a zolemera zace za Davide.
32 Ndipo Yonatani atate wace wina wa Davide anali phungu, munthu wanzeru ndi mlembi; ndi Yehieli mwana wa Hakimoni anakhala ndi ana a mfumu;
33 ndi Ahitofeli anali phungu wa mfumu, ndi Husai M-ariki anali bwenzi la mfumu;