1 Ana a Yuda: Perezi, Hezroni, ndi Karmi, ndi Huri, ndi Sobala.
2 Ndipo Reaya mwana wa Sobala anabala Yahati; ndi Yahati anabala Ahumai, ndi Lahadi. Iwo ndiwo mabanja a Azorati.
3 Iwo ndiwo a atate wa Etamu: Yezreeli, ndi Isma, ndi Idibasi; ndipo dzina la mlongo wao ndiye Hazeleleponi,
4 ndi Penueli atate wa Gedoro, ndi Ezeri atate wa Husa. Awa ndi ana a Huri woyamba wa Efrata atate wa Betelehemu.
5 Ndipo Asuri atate wa Tekowa anali nao akazi awiri: Hela, ndi Naara.