8 ndi Ibineya mwana wa Yerohamu, ndi Ela mwana wa Uzi, mwana-wa Mikiri, ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli, mwana wa Ibniya,
9 ndi abale ao monga mwa mibadwo yao mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi. Onsewa ndiwo akuru a nyumba za makolo ao m'nyumba za makolo ao.
10 Ndi a ansembe: Yedaya, ndi Yehoyaribu, ndi Yakini,
11 ndi Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubu, mtsogoleri wa m'nyumba ya Mulungu;
12 ndi Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasuri, mwana wa Malikiya, ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yazera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemiti, mwana wa Imeri,
13 ndi abale ao, akuru a nyumba za makolo ao cikwi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi limodzi, anthu odziwitsitsa Debito ya utumiki wa nyumba ya Mulungu.
14 Ndi a Alevi: Semaya mwana wal Hasubu, mwana wa Azrikamu, mwana wa Hasabiya, a ana a Merari;