1 Pamenepo Samueli anatenga nsupa ya mafuta, nawatsanulira pamutu pace, nampsompsona iye, nati, Sanakudzozani ndi Mulungu kodi, mukhale mfumu ya pa colowa cace?
2 M'mene talekana lero, mudzakomana ndi anthu awiri pa manda a Rakele, pa malire a Benjamini ku Zeliza; iwo ndiwo adzanena nanu, Aburu aja munakafuna, anapezedwa; ndipo onani, atate wanu analeka kulingalira aburuwo, koma alikulingalira za inu, ndi kuti, Ndidzacita ciani, cifukwa ca mwana wanga?
3 Mukapitirira pamenepo tsono ndi kufika ku mtengo wathundu wa ku Tabori, kumeneko adzakomana nanu anthu atatu akukwera kwa Mulungu ku Beteli, wina wonyamula ana a mbuzi atatu, wina mikate itatu, wina thumba la vinyo.
4 Iwowa adzakulankhulani, ndi kukupatsani mikate iwiri; imeneyi mudzailandira m'manja mwao.