14 Ndipo Davide anakhala wocenjera m'mayendedwe ace onse; ndipo Yehova anali naye.
15 Ndipo pamene Sauli anaona kuti analikukhala wocenjera ndithu anamuopa.
16 Koma Aisrayeli onse ndi Ayuda onse anamkonda Davide pakuti anawatsogolera kuturuka ndi kulowa nao.
17 Ndipo Sauli anati kwa Davide, Ona, mwana wanga wamkazi wamkuru, dzina lace Merabi, iyeyo ndidzakupatsa akhale mkazi wako; koma undikhalire ngwazi, nuponye nkhondo za Yehova. Pakuti Sauli anati, Dzanja langa lisamkhudze, koma dzanja la Afilisti ndilo.
18 Ndipo Davide anati kwa Sauli, Ine ndine yani, ndi moyo wanga uli wotani, kapena banja la atate wanga liri lotani m'Israyeli, kuti ine ndidzakhala mkamwini wa mfumu?
19 Koma kunali nthawi imene akadapatsa Merabi mwana wamkazi wa Sauli kwa Davide, iye anapatsidwa kwa Adrieli Mholati kukhala mkazi wace.
20 Ndipo Mikala mwana wamkazi wa Sauli anakonda Davide; ndipo pakumva Sauli, anakondwera nako.