1 Ndipo Hana anapemphera, natiMtima wanga umyuka mokondwera kwa Yehova,Nyanga yanga yakwezeka mwa Yehova;Pakamwa panga pakula kwa adani anga;Popeza ndikondwera m'cipulumutsocanu.
2 Palibe wina woyera ngati Yehova;Palibe wina koma Inu nokha;Palibenso thanthwe longa Mulungu wathu.
3 Musalankhulenso modzikuza kwambiri motero;M'kamwa mwanu musaturuke zolulutsa;Cifukwa Yehova ali Mulungu wanzeru,Ndipo iye ayesa zocita anthu.
4 Mauta a amphamvu anathyoka,Koma okhumudwawo amangiridwa ndi mphamvu m'cuuno.
5 Amene anakhuta anakasuma cakudya;Koma anjalawo anacira;Inde cumba cabala asanu ndi awiri:Ndipo iye amene ali ndi ana ambiri acita liwondewonde.
6 Yehova amapha, napatsa moyo:Iye amatsitsa kumanda, naukitsanso.
7 Yehova asaukitsa, nalemeza;Acepetsa, nakuzanso.