21 Ndipo Yehova anakumbukila Hana, naima iye, nabala ana amuna atatu, ndi ana akazi awiri. Ndipo mwanayo Samueli anakula pamaso pa Yehova.
22 Ndipo Eli anali wokalamba ndithu; namva zonse ana ace anacitira Aisrayeli onse, ndi kuti anagona ndi akazi akusonkhana pa khomo la cihema cokomanako.
23 Ndipo iye ananena nao, Mumacitiranji zotere? popeza ndirinkumva za macitidwe anu oipa kwa anthu onsewa.
24 Iai, ana anga, popeza mbiri imene ndirikuimva siri yabwino iai; mulikulakwitsa anthu a Yehova.
25 Munthu akacimwira munthu mnzace oweruza adzaweruza mrandu wace; koma ngati munthu acimwira Yehova, adzampembedzera ndani? Koma ngakhale adatero, iwo aja anakhalabe osamvera mau a atate wao, cifukwa Yehova adati adzawaononga.
26 Ndipo mwanayo Samueli anakulakula, ndipo Yehova ndi anthu omwe anamkomera mtima.
27 Ndipo anafika kwa Eli munthu wa Mulungu, nanena naye, Atero Yehova, Kodi Ine ndinadziulula kwa banja la kholo lako, muja anali m'Aigupto, m'nyumba ya Farao?