12 Ndipo Davide anasunga mau awa mumtima mwace, naopa kwambiri Akisi mfumu ya Gati.
13 Nasanduliza makhalidwe ace pamaso pao, nadzionetsera m'manja mwao ngati wamisala, nangolembalemba pa zitseko za cipata, nakhetsa dobvu lace pa ndebvu yace.
14 Tsono Akisi ananena ndi anyamata ace, Taonani, mupenya kuti munthuyo ngwa misala; mwabwera naye kwa ine cifukwa ninji?
15 Kodi ndisowa anthu amisala kuti mwabwera ndi uyu kuti akhale wamisala pamaso panga? Kodi uyu adzalowa m'nyumba mwanga?