19 Nati kwa anyamataace, Nditsogolereni; onani ndidza m'mbuvo mwanu. Koma sanauza mwamuna wace Nabala.
20 Ndipo kudatero pakuberekeka iye pa buru wace, natsikira pa malo obisika a m'phirilo, onani, Davide ndi anthu ace analikutsikira kwa iye; iye nakomana nao.
21 Koma Davide adanena, Zoonadi ndasunga cabe zace zonse za kaja kanali nazo m'cipululu, sikadasowa kanthu ka zace zonse; ndipo iye anandibwezera zoipa m'malo mwa zabwino.
22 Mulungu alange adani a Davide, ndi kuonjezerapo, ngati ndisiyapo kufikira kuunika kwa m'mawa, kanthu konse ka iye, kangakhale kamwana kamphongo.
23 Ndipo Abigayeli pakuona Davide, anafulumira kutsika pa bum, nagwa pamaso pa Davide nkhope yace pansi, namgwadira,
24 Ndipo atagwadira pa mapazi ace anati, Pa ine, mbuye wanga, pa ine pakhale ucimowo; ndipo mulole mdzakazi wanu alankhule m'makutu anu, nimumvere mau a mdzakazi wanu.
25 Mbuye wanga, musasamalire munthu uyu woipa, ndiye Nabala; cifukwa monga dzina lace momwemo iye; dzina lace ndiye Nabala, ndipo ali nako kupusa; koma ine mdzakazi wanu sindinaona anyamata a mbuye wanga, amene munawatumiza.