15 Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Wandibvutiranji kundikweretsa kuno? Sauli nayankha, Ndirikusautsika kwambiri, pakuti Afilisti aponyana nkhondo ndi ine, ndipo Mulungu anandicokera, osandiyankhanso, kapena ndi aneneri, kapena ndi maloto; cifukwa cace ndakuitanani, kuti mundidziwitse cimene ndiyenera kucita.