8 Popeza nyumba yonse ya Ahabu idzaonongeka, ndipo ndidzalikhira Ahabu ana amuna onse womangika ndi womasuka m'Israyeli.
9 Ndipo ndidzalinganiza nyumba ya Ahabu ndi nyumba ya Yerobiamu mwana wa Nebati, ndi nyumba ya Basa mwana wa Ahiya.
10 Ndipo agaru adzamudya Yezebeli pa dera la Yezreeli, wopanda wina wakumuika. Pamenepo anatsegula pakhomo, nathawa.
11 Ndipo Yehu anaturukira kwa anyamata a mbuye wace, nanena naye wina, Mtendere kodi? anakudzera cifukwa ninji wamisala uyu? Nanena nao, Mumdziwa munthuyo ndi makambidwe ace.
12 Nati iwo, Kunama uku; utifotokozere tsono. Nati iye, Anati kwa ine cakuti cakuti; ndi kuti, Atero Yehova, Ndakudzoza mfumu pa Israyeli.
13 Nafulumira iwo, nagwira yense copfunda cace, naciyala pokhala iye paciunda, naomba lipenga, nati, Yehu ndiye mfumu.
14 Motero Yehu mwana wa Yehosafati mwana wa Nimsi anapandukira Yoramu. Tsono Yoramu atalindira ku Ramoti Gileadi, iye ndi Aisrayeli onse, cifukwa ca Hazaeli mfumu ya Aramu;