11 Munandibveka khungu ndi mnofu,Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,
12 Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.
13 Koma izi munazibisa mumtima mwamu;Ndidziwa kuti ici muli naco:
14 Ndikacimwa mundipenya;Ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.
15 Ndikakhala woipa, tsoka ine;Ndikakhala wolungama, sindidzakweza mutuwanga;Ndadzazidwa ndi manyazi, Koma penyani kuzunzika kwanga.
16 Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango;Mubweranso ndi kudzionetsera modabwiza kwa ine.
17 Mundikonzeranso mboni zonditsutsa,Ndi kundicurukitsira mkwiyo wanu;Nkhondo yobwereza-bwereza yandigwera.