Yobu 37 BL92

1 Pa icinso mtima wanga unienjemera,Nusunthika m'malo mwace.

2 Mvetsetsani cibumo ca mau ace,Ndi kugunda koturuka m'kamwa mwace.

3 Akumveketsa pansi pa thambo ponse,Nang'anipitsa mphezi yace ku malekezero a dziko lapansi.

4 Mau abuma kuitsata,Agunda ndi mau a ukulu wace,Ndipo sailetsa atamveka mau ace,

5 Mulungu agunda modabwitsa ndi mau ace,Acita zazikuru osazidziwa ife.

6 Pakuti anena kwa cipale cofewa, Ugwe padziko.Momwemonso kwa mvula,Ndi kwa mbvumbi waukuru.

7 Atsekereza mokhomera cizindikilo dzanja la munthu ali yense,Kuti anthu onse anawalenga adziwe.

8 Pamenepo zirombo zilowa mobisalamo,Nizikhala m'ngaka mwao.

9 M'cipinda mwace muturuka kabvumvulu,Ndi cisanu cifuma kumpoto.

10 Mwa kupuma kwace apereka cipale,Ndi madzi acitando aundana.

11 Asenzetsanso mtambo wakuda bii madzi,Afunyulula mtambo wokhalamo mphezi yace;

12 Ndipo utembenuka-tembenuka pakulangiza kwace,Kuti ucite ziri zonse aulamulira,Pa nkhope ya dziko lokhalamo anthu;

13 Ngati aufikitsira dziko lace kulidzudzula,Kapena kulicitira cifundo.

14 Tamverani ici, Yobu.Taimani, mulingirire zodabwiza za Mulungu.

15 Kodi mudziwa umo Mulungu azilangizira zimenezi,Nawalitsa mphezi ya m'mtambo mwace?

16 Kodi mudziwa madendekeredwe ace a mitambo,Zodabwiza za Iye wakudziwa mwangwiro?

17 Kodi mudziwa umo zobvala zanu zifundira,Pamene dziko liri thuu cifukwa ca mwela?

18 Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye,Ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?

19 Mutilangize cimene tidzanena ndi Iye;Sitidziwa kulongosola mau athu cifukwa ca mdima.

20 Kodi munthu ayenera kumuuza kuti ndifuna kunena,Kapena kodi munthu adzakhumba kumezedwa?

21 Ndipo tsopano anthu sakhoza kupenyerera kuunika pakunyezimira kuthambo,Ndi mphepo yapita ndi kuuyeretsa,

22 Kucokera kumpoto kudzera kuwala konyezimira,Mulungu ali nao ukulu woopsa.

23 Kunena za Wamphamvuyonse, sitingamsanthule; ndiye wa mphamvu yoposa;Koma mwa ciweruzo ndi cilungamo cocuruka samasautsa.

24 M'mwemo anthu amuopa,Iye sasamalira ali yense wanzeru mumtima.