Yobu 30 BL92

1 Koma tsopano iwo osafikana msinkhu wanga andiseka,Iwo amene atate ao ndikadawapeputsa, osawaika pamodzi ndi agaru olinda nkhosa zanga.

2 Mphamvunso ya m'manja mwao ndikadapindulanji nayo?Ndiwo anthu amene unyamata wao udatha,

3 Atsala mafupa okha okha ndi kusowa ndi njala;Akungudza nthaka youma kuli mdima wa m'cipululu copasuka.

4 Achera terere lokolera kuzitsamba,Ndi cakudya cao ndico mizu ya dinde.

5 Anawapitikitsa pakati pa anthu,Awapfuulira ngati kutsata mbala.

6 Azikhala m'zigwa za cizirezire,M'maenje a m'nthaka ndi m'mapanga.

7 Pakati pa zitsamba alira ngati buru,Pansi pa khwisa asonkhana pamodzi.

8 Ndiwo ana a opusa, inde ana a anthu opanda dzina;Anawaingitsa kuwacotsa m'dziko.

9 Koma tsopano ndasanduka nyimbo ya oterewo,Nandiyesa nthanthi.

10 Anyansidwa nane, akhala patali ndi ine,Saleka kuthira malobvu pankhope panga.

11 Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza;Anataya comangira m'kamwa mwao pamaso panga.

12 Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka,Akankha mapazi anga,Andiundira njira zao zakundiononga.

13 Aipsa njira yanga,Athandizana ndi tsoka langa;Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.

14 Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru,Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.

15 Anditembenuzira zondiopsa,Auluza ulemu wanga ngati mphepo;Ndi zosungika zanga zapita ngati mtambo.

16 Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga;Masiku akuzunza andigwira.

17 Nyengo ya usiku mafupa anga awaza mwa ine,Ndi zowawa zondikungudza sizipuma.

18 Mwa mphamvu yaikuru ya nthenda yanga cobvala canga cinasandulika,Cindithina ngati pakhosi pa maraya anga.

19 Iye anandiponya m'matope,Ndipo ndafanana ndi pfumbi ndi phulusa.

20 Ndipfuula kwa Inu, koma simundiyankha;Ndinyamuka, ndipo mungondipenyerera.

21 Mwasandulika kundicitira nkharwe;Ndi mphamvu ya dzanja lanu mundizunza.

22 Mundikweza kumphepo, mundiyendetsa pomwepo;Ndipo mundisungunula mumkuntho.

23 Pakuti ndidziwa kuti mudzandifikitsa kuimfa,Ndi ku nyumba yokomanamo amoyo onse.

24 Koma munthu akati agwe, satambasula dzanja lace kodi?Akati aonongeke, sapfuulako kodi?

25 Kodi sindinamlirira misozi wakulawa zowawa?Kodi moyo wanga sunacitira cisoni osowa?

26 Muja ndinayembekeza cokoma cinadza coipa,Ndipo polindira kuunika unadza mdima.

27 M'kati mwanga mupweteka mosapuma,Masiku a mazunzo andidzera.

28 Ndiyenda ndiri wothimbirira osati ndi dzuwa ai;Ndinyamuka mumsonkhano ndi kupfuula,

29 Ndiri mbale wao wa ankhandwe,Ndi mnansi wao wa nthiwatiwa.

30 Khungu langa lada, nilindipfundukira;Ndi mafupa anga awawa ndi kutentha kwao.