14 Ndikacimwa mundipenya;Ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.
15 Ndikakhala woipa, tsoka ine;Ndikakhala wolungama, sindidzakweza mutuwanga;Ndadzazidwa ndi manyazi, Koma penyani kuzunzika kwanga.
16 Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango;Mubweranso ndi kudzionetsera modabwiza kwa ine.
17 Mundikonzeranso mboni zonditsutsa,Ndi kundicurukitsira mkwiyo wanu;Nkhondo yobwereza-bwereza yandigwera.
18 Potero munandibadwitsa cifukwa ninji?Mwenzi nditapereka moyo wanga, lisanandione diso.
19 Ndikadakhala monga ngati sindikadakhala;Akadanditenga pobadwapo kumka nane kumanda.
20 Masiku anga satsala owerengeka nanga? lindani,Bandilekani kuti nditsitsimuke pang'ono,