2 Ndidzati kwa Mulungu, Musanditsutse;Mundidziwitse cifukwa ca kutsutsana nane.
3 Cikukomerani kodi kungosautsa,Kuti mupeputsa nchito yolemetsa manja anu,Ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?
4 Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?
5 Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;
6 Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;
7 Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?
8 Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.