4 Muli nao maso a thupi kodi?Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?
5 Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,Zaka zanu zikunga masiku a munthu;
6 Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;
7 Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?
8 Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.
9 Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?
10 Simunanditsanula kodi ngati mkaka,Ndi kundilimbitsa ngati mase?