6 Kuti mufunsa mphulupulu yanga,Ndi kulondola coipa canga;
7 Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa,Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?
8 Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.
9 Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?
10 Simunanditsanula kodi ngati mkaka,Ndi kundilimbitsa ngati mase?
11 Munandibveka khungu ndi mnofu,Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,
12 Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.