8 Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,Koma mufuna kundiononga.
9 Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi;Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?
10 Simunanditsanula kodi ngati mkaka,Ndi kundilimbitsa ngati mase?
11 Munandibveka khungu ndi mnofu,Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,
12 Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.
13 Koma izi munazibisa mumtima mwamu;Ndidziwa kuti ici muli naco:
14 Ndikacimwa mundipenya;Ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.