9 Muyeso wace utalikira utali wace wa dziko lapansi,Citando cace ciposa ca nyanja.
10 Akapita, nakatsekera,Nakaturutsa bwalo la mlandu, adzamletsa ndani?
11 Pakuti adziwa anthu opanda pace,Napenyanso mphulupulu, ngakhale saisamalira.
12 Koma munthu wopanda pace asowa nzeru,Ngakhale munthu abadwa ngati mwana wa mbidzi.
13 Ukakonzeratu mtima wako,Ndi kumtambasulira Iye manja ako;
14 Mukakhala mphulupulu m'dzanja lako, uicotseretu kutali,Ndi cisalungamo cisakhale m'mahema mwako;
15 Popeza pamenepo udzakweza nkhope yako opanda banga;Nudzalimbika osacita mantha;