10 Adzakudzudzulani ndithu,Mukacita tsankhu m'tseri.
11 Ukulu wace sukucititsani mantha,Ndi kuopsa kwace sikukugwerani kodi?
12 Zikumbutso zanu ndizo miyambi ya mapulusa;Zodzikanira zanu zikunga malinga adothi.
13 Khalani cete, ndilekeni, kuti ndinene,Condifikira cifike.
14 Ndilumirenji mnofu wanga pamano panga,Ndi kupereka moyo wanga m'dzanja langa?
15 Angakhale andipha koma ndidzamlindira;Komanso ndidzaumirira mayendedwe anga pamaso pace.
16 Iye adzakhalanso cipulumutso canga,Pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pace.