15 Angakhale andipha koma ndidzamlindira;Komanso ndidzaumirira mayendedwe anga pamaso pace.
16 Iye adzakhalanso cipulumutso canga,Pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pace.
17 Mvetsetsani mau anga,Ndi kunenetsa kwanga kumveke m'makutu mwanu.
18 Taonani tsono, ndalongosola mlandu wanga;Ndidziwa kuti adzandimasula ndiri wolungama,
19 Ndaniyo adzatsutsana nane?Ndikakhala cete, ndidzapereka mzimu wanga.
20 Zinthu ziwiri zokha musandicitire,Pamenepo sindidzabisalira nkhope yanu:
21 Mundicotsere dzanja lanu kutali,Ndi kuopsa kwanu kusandicititse mantha.