17 Mvetsetsani mau anga,Ndi kunenetsa kwanga kumveke m'makutu mwanu.
18 Taonani tsono, ndalongosola mlandu wanga;Ndidziwa kuti adzandimasula ndiri wolungama,
19 Ndaniyo adzatsutsana nane?Ndikakhala cete, ndidzapereka mzimu wanga.
20 Zinthu ziwiri zokha musandicitire,Pamenepo sindidzabisalira nkhope yanu:
21 Mundicotsere dzanja lanu kutali,Ndi kuopsa kwanu kusandicititse mantha.
22 Pamenepo muitane, ndipo ndidzayankha;Kapena ndinene ndine, ndipo mundiyankhe ndinu.
23 Mphulupulu zanga ndi zocimwa zanga ndi zingati?Mundidziwitse kulakwa kwanga ndi cimo langa,