25 Kodi mudzaopsa tsamba lakungouluka,Ndi kulondola ziputu zouma?
26 Pakuti mundilembera zinthu zowawa,Ndi kundipatsa ngati colowa mphulupulu za ubwana wanga.
27 Mulonganso mapazi anga m'zigologolo, ndi kupenyerera mayendedwe anga onse;Mudzilembera malire mopanika mapazi anga;
28 Momwemo munthu akutha ngati cinthu coola,Ngati cobvala codyedwa ndi numbi