3 Koma ine ndidzanena ndi Wamphamvuyonse,Ndipo ndifuna kudzikanira kwa Mulungu.
4 Koma inu ndinu opanga zabodza,Asing'anga opanda pace inu nonse.
5 Mwenzi mutakhala cete konse,Ndiko kukadakhala nzeru zanu.
6 Tamvani tsono kudzikanira kwanga,Tamverani kudzinenera kwa milomo yanga.
7 Kodi munenera Mulungu mosalungama,Ndi kumnenera Iye monyenga?
8 Kodi mukhalira kumodzi ndi Iye?Mundilimbirana mwa Mulungu.
9 Ncokoma kodi kuti Iye akusanthuleni?Kodi mudzamnyenga Iye monga munyenga munthu?