7 Kodi munenera Mulungu mosalungama,Ndi kumnenera Iye monyenga?
8 Kodi mukhalira kumodzi ndi Iye?Mundilimbirana mwa Mulungu.
9 Ncokoma kodi kuti Iye akusanthuleni?Kodi mudzamnyenga Iye monga munyenga munthu?
10 Adzakudzudzulani ndithu,Mukacita tsankhu m'tseri.
11 Ukulu wace sukucititsani mantha,Ndi kuopsa kwace sikukugwerani kodi?
12 Zikumbutso zanu ndizo miyambi ya mapulusa;Zodzikanira zanu zikunga malinga adothi.
13 Khalani cete, ndilekeni, kuti ndinene,Condifikira cifike.