12 Ndinali mkupuma, koma anandityola;Inde anandigwira pakhosi, nandiphwanya;Anandiimika ndikhale candamali.
13 Eni mauta ace andizinga,Ang'amba imso zanga, osazileka;Natsanulira pansi ndulu yanga.
14 Andipasula-pasula;Andithamangira ngati wamphamvu.
15 Ndadzisokerera ciguduli ku khungu langa,Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m'pfumbi.
16 Nkhope yanga njodetsedwa ndi kulira misozi,Ndi pa zikope zanga pali mthunzi wa imfa;
17 Pangakhale palibe ciwawa m'manja mwanga,Ndi pemphero langa ndi loyera.
18 Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga,Ndi kulira kwanga kusowe popumira.