19 Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba,Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.
20 Mabwenzi anga andinyoza; Koma diso langa lilirira misozi kwa Mulungu;
21 Ha! munthu akadapembedzera mnzace kwa Mulungu,Monga munthu apembedzera mnansi wace!
22 Pakuti zitafika zaka zowerengeka,Ndidzamuka ku njira imene sindibwererako.