3 Kodi adzatha mau ouluzika?Kapena cikuwindula nciani kuti uyankha zotere?
4 Inenso ndikadanena monga inu,Moyo wanu ukadakhala m'malo mwa moyo wanga,Ndikadalumikizanitsa mau akutsutsana nanu,Ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 Koma ndikadakulimbikitsani ndi m'kamwa mwanga,Ndi citonthozo ca milomo yanga cikadatsitsa cisoni canu.
6 Cinkana ndinena cisoni canga sicitsika;Ndipo ndikaleka, cindicokera nciani?
7 Koma tsopano wandilemetsa Iye;Mwapasula msonkhano wanga wonse.
8 Kundigwira kwanu, ndiko umboni wonditsutsa,Kuonda kwanga kundiukira, kucita umboni pamaso panga.
9 Iye ananding'amba m'kundida kwace, nakwiya nane,Anandikukutira mano;Mdani wanga ananditong'olera maso ace.