1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,
2 Musaka mau kufikira liti?Zindikirani, ndi pamenepo tidzanena.
3 Tiyesedwa bwanji ngati nyama za kuthengo,Ndi kukhala odetsedwa pamaso panu?
4 Iwe wodzing'amba mumkwiyo mwako,Kodi dziko lapansi lisiyidwe cifukwa ca iwe?Kapena thanthwe lisunthike m'malo mwace?