6 Kuunikaku kudzada m'hema mwace,Ndi nyali yace ya pamwamba pace idzazima.
7 Mapondedwe ace amphamvu adzasautsidwa,Ndi uphungu wace wace udzamgwetsa.
8 Pakuti aponyedwa m'ukonde ndi mapazi ace,Namaponda pamatanda.
9 Msampha udzamgwira kucitende,Ndi khwekhwe lidzamkola.
10 Msampha woponda umbisikira pansi,Ndi msampha wa cipeto panjira.
11 Zoopetsa zidzamcititsa mantha monsemo,Nadzampitikitsa kumbuyo kwace.
12 Njala idzatha mphamvu yace,Ndi tsoka lidzamkonzekeratu pambali pace.