7 Mapondedwe ace amphamvu adzasautsidwa,Ndi uphungu wace wace udzamgwetsa.
8 Pakuti aponyedwa m'ukonde ndi mapazi ace,Namaponda pamatanda.
9 Msampha udzamgwira kucitende,Ndi khwekhwe lidzamkola.
10 Msampha woponda umbisikira pansi,Ndi msampha wa cipeto panjira.
11 Zoopetsa zidzamcititsa mantha monsemo,Nadzampitikitsa kumbuyo kwace.
12 Njala idzatha mphamvu yace,Ndi tsoka lidzamkonzekeratu pambali pace.
13 Zidzatha ziwalo za thupi lace,Mwana woyamba wa imfa adzatha ziwalo zace.