1 Koma Yobu anayankha, nati,
2 Mudzasautsa moyo wanga kufikira liti,Ndi kundityolatyola nao mau?
3 Kakumi aka mwandicititsa manyazi;Mulibe manyazi kuti mundiumira mtima.
4 Ndipo ngati ndalakwa ndithu,Kulakwa kwanga kuli ndi ine ndekha.