13 Iye anandicotsera abale anga kutali,Ndi odziwana nane andiyesa mlendo konse.
14 Anansi anga andisowa,Ndi odziwana nane bwino andiiwala.
15 Iwo a m'nyumba mwanga ndi adzakazi anga andiyesa mlendo;Ndine wacilendo pamaso pao.
16 Ndikaitana kapolo wanga, sandibwezera mau,Cinkana ndimpembedza pakamwa panga.
17 Mpweya wanga unyansira mkazi wanga,Cinkana ndinampembedza ndi kuchula ana a thupi langa.
18 Angakhale ana ang'ono andipeputsa,Ndikanyamuka, andinena;
19 Mabwenzi anga eni eni onse anyansidwa nane;Ndi onse ndakondana nao asandulika adani anga.