2 Mudzasautsa moyo wanga kufikira liti,Ndi kundityolatyola nao mau?
3 Kakumi aka mwandicititsa manyazi;Mulibe manyazi kuti mundiumira mtima.
4 Ndipo ngati ndalakwa ndithu,Kulakwa kwanga kuli ndi ine ndekha.
5 Ngati inu mudzikuza ndithu pa ine,Ndi kundichulira mtonzo wanga kuti munditsutse nao;
6 Dziwani tsopano kuti Mulungu wandikhotetsera mlandu wanga,Nandizinga ndi ukonde wace.
7 Taonani, ndipfuula kuti, Ciwawa! koma sandimvera;Ndikuwa, koma palibe ciweruzo.
8 Iye ananditsekera njira kuti ndisapitireko,Naika mdima poyendapo ine.