20 Pfupa langa laumirira pa khungu langa ndi mnofu wanga,Ndipo ndapulumuka ndiri nazo nkhama za mano anga.
21 Ndicitireni cifundo, ndicitireni cifundo, mabwenzi anga inu;Pakuti dzanja la Mulungu landikhudza.
22 Mundilondola bwanji ngati Mulungu,Losakukwanirani thupi langa?
23 Ha! akadalembedwa mau anga!Ha! akadalembedwa m'buku!
24 Akadawazokota pathanthwe cikhalire,Ndi cozokotera cacitsulo ndi kuthira ntobvu!
25 Koma ndidziwa kuti Mombolo wanga ali ndi moyo,Nadzauka potsiriza papfumbi.
26 Ndipo khungu langa litaonongeka,Pamenepo wopanda thupi langa, ndidzapenya Mulungu;