22 Ngati pali munthu wakumphunzitsa Mulungu nzeru?Popeza Iye aweruza mlandu iwo okwezeka.
23 Wina akufa, wabiriwiri,Ali cikhalire ndi cipumulire.
24 Mbale zace zidzala ndi mkaka;Ndi wongo wa m'mafupa ace uli momwe.
25 Koma mnzace akufa ali nao mtima wakuwawa,Osalawa cokoma konse.
26 Iwo agona cimodzimodzi kupfumbi,Ndi mphutsi ziwakuta.
27 Taonani, ndidziwa maganizo anu,Ndi ciwembu mundilingirira moipa,
28 Pakuti munena, Iri kuti nyumba ya kalonga?Ndi hema wokhalamo woipa ali kuti?