3 Mundilole, ndinene nanenso; Ndipo nditanena ine, sekani.
4 Kodi ine, kudandaula kwanga, ndidandaulira munthu?Ndipo ndilekerenji kupsa mtima?
5 Ndiyang'anireni, nimusumwe,Gwirani pakamwa panu.
6 Ndikangokumbukila ndibvutika mtima,Ndi thupi langa licita nyau nyau.
7 Oipa akhaliranji ndi moyo,Nakalamba, nalemera kwakukuru?
8 Mbeu zao zikhazikika pamodzi nao pankhope pao,Ndi ana ao pamaso pao,
9 Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha,Ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.