7 Oipa akhaliranji ndi moyo,Nakalamba, nalemera kwakukuru?
8 Mbeu zao zikhazikika pamodzi nao pankhope pao,Ndi ana ao pamaso pao,
9 Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha,Ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.
10 Ng'ombe yao yamphongo imakwera, yosakanika;Ng'ombe yao yaikazi imaswa, yosapoloza.
11 Aturutsa makanda ao ngati gulu,Ndi ana ao amabvinabvina.
12 Ayimbira lingaka ndi zeze,Nakondwera pomveka citoliro.
13 Atsekereza masiku ao ndi zokoma,Natsikira m'kamphindi kumanda.