11 Kapena mdima kuti ungaone,Ndi madzi aunyinji akumiza.
12 Kodi Mulungu sakhala m'mwamba m'tali?Ndipo penyani kutalika kwace kwa nyenyezi, ziri m'talitali.
13 Ndipo ukuti, Adziwa ciani Mulungu?Aweruza kodi mwa mdima wa bii?
14 Mitambo ndiyo comphimba, kuti angaone;Ndipo amayenda pa thambo lakumwamba.
15 Udzasunga kodi njira yakale,Anaiponda anthu amphulupulu?
16 Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao,Cigumula cinakokolola kuzika kwao;
17 Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni;Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?