12 Kodi Mulungu sakhala m'mwamba m'tali?Ndipo penyani kutalika kwace kwa nyenyezi, ziri m'talitali.
13 Ndipo ukuti, Adziwa ciani Mulungu?Aweruza kodi mwa mdima wa bii?
14 Mitambo ndiyo comphimba, kuti angaone;Ndipo amayenda pa thambo lakumwamba.
15 Udzasunga kodi njira yakale,Anaiponda anthu amphulupulu?
16 Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao,Cigumula cinakokolola kuzika kwao;
17 Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni;Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?
18 Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino;Koma uphungu wa oipa unditalikira.