16 Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao,Cigumula cinakokolola kuzika kwao;
17 Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni;Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?
18 Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino;Koma uphungu wa oipa unditalikira.
19 Olungama aciona nakondwera; Ndi osalakwa awaseka pwepwete,
20 Ndi kuti, Zoonadi, otiukirawo alikhidwa,Ndi zowatsalira, moto unazipsereza.
21 Uzolowerane ndi Iye, nukhale ndi mtendere;Ukatero zokoma zidzakudzera,
22 Landira tsono cilamulo pakamwa pace,Nuwasunge maneno ace mumtimamwako.