4 Kodi akudzudzula, nadza nawe kumlandu,Cifukwa ca kumuopa kwako?
5 Zoipa zako sizicuruka kodi?Ndi mphulupulu zako sizikhala zosawerengeka kodi?
6 Pakuti wamtenga cikole kwa mbale wako wopanda cifukwa,Ndi kubvula ausiwa zobvala zao.
7 Sunampatsa wolema madzi amwe,Ndi wanjala unammana cakudya.
8 Koma munthu mwini mphamvu, dziko ndi lace;Ndi munthu wobvomerezeka, anakhala momwemo.
9 Unabweza akazi amasiye osawaninkha kanthu,Ndi manja a ana amasiye anatyoledwa.
10 Cifukwa cace misampha ikuzinga.Ndi mantha akubvuta modzidzimutsa,