7 Agona amarisece usiku wonse opanda cobvala,Alibe copfunda pacisanu.
8 Abvumbwa ndi mvula kumapiri,Nafukata thanthwe posowa pousapo.
9 Akwatula wamasiye kubere,Natenga cikole cobvala ca osauka;
10 Momwemo ayenda amarisece opanda cobvala,Nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.
11 M'kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta;Aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.
12 M'mudzi waukuru anthu abuula alinkufa;Ndi moyo wa iwo olasidwa upfuula;Koma Mulungu sasamalira coipaco.
13 Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,Sadziwa njira zace,Sasunga mayendedwe ace.