12 Taonani, inu nonse munaciona;Ndipo mugwidwa nazo zopanda pace cifukwa ninji?
13 Ili ndi gawo la munthu woipa kwa Mulungu,Ndi colowa ca akupsinja anzao acilandira kwa Wamphamvtiyonse.
14 Akacuruka ana ace, ndiko kucurukira lupanga,Ndi ana ace sadzakhuta cakudya.
15 Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa,Ndi akazi ace amasiye sadzalira maliro.
16 Cinkana akundika ndalama ngati pfumbi,Ndi kukonzeratu zobvala ngati dothi;
17 Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.
18 Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.