14 Akacuruka ana ace, ndiko kucurukira lupanga,Ndi ana ace sadzakhuta cakudya.
15 Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa,Ndi akazi ace amasiye sadzalira maliro.
16 Cinkana akundika ndalama ngati pfumbi,Ndi kukonzeratu zobvala ngati dothi;
17 Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala,Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.
18 Amanga nyumba yace ngati kadzoce,Ndi ngati wolindira amanga dindiro.
19 Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa;Potsegula maso ace, wafa cikomo,
20 Zoopsa zimgwera ngati madzi;Nkuntho umtenga usiku.