7 Mdani wanga akhale ngati woipa,Ndi iye amene andiukira ngati wosalungama.
8 Pakuti ciyembekezo ca wonyoza Mulungu nciani pomlikhatu Mulungu,Pomcotsera moyo wace?
9 Kodi Mulungu adzamvera kupfuula kwace, ikamdzera nsautso?
10 Kodi adzadzikondweretsa naze Wamphamvuyonse,Ndi kuitana kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Ndidzakulangizani za dzanja la Mulungu;Cokhala ndi Wamphamvuyonse sindidzacibisa.
12 Taonani, inu nonse munaciona;Ndipo mugwidwa nazo zopanda pace cifukwa ninji?
13 Ili ndi gawo la munthu woipa kwa Mulungu,Ndi colowa ca akupsinja anzao acilandira kwa Wamphamvtiyonse.