1 Koma kuli mtapo wa siliva, Ndi malo a golidi amene amuyenga.
2 Citsulo acitenga m'nthaka,Ndi mkuwa ausungunula kumwala.
3 Munthu athawitsa mdima,Nafunafuna mpaka malekezero onse,Miyala ya mdima wa bii ndi ya mthunzi wa imfa.
4 Aboola mgodi posiyana patali pokhala anthu;Aiwalika ndi phazi lopitapo;Apacikika kutali ndi anthu, nalendewa-lendewa.