25 Pamene anaikira mphepo muyeso wace,Nayesera madzi miyeso;
26 Pakucitira mvula lamulo,Ndi njira yoyendamo mphezi ya bingu;
27 Pamenepo anaiona nzeru, naifotokozera;Anaikonza, naisanthula.
28 Koma kwa munthu anati,Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru;Ndi kupatukana naco coipa ndiko luntha.